Owaganizira Kupha Awamanga

Apolisi amanga abambo atatu - a Gift Banda a zaka 29, a Yusuf Matola a zaka 33 ndi a Regan Phiri a zaka 39 - powaganizira kuti akukhudzidwa ndi kuphedwa kwa mzika ya dziko la South Korea pa 7 February chaka chino.

Mzikayo, a Woonja Hwang, inaphedwa pafupi ndi mtsinje wa Lilongwe pomwe imapita kukaphunzira masewero a tenisi ku bwalo la Lilongwe Golf Club.

Anthuwa akuwaganiziranso kuti anaba lamya ya m’manja ya malemuwo.

Wachiwiri kwa mneneri wa apolisi m'dziko lino Superintendent Alfred Chimthere watiuza kuti anthuwa akaonekera m’bwalo la milandu posachedwapa, kukayankha mlandu wokupha.

Read 1994 times

Last modified on Wednesday, 13/03/2024

Login to post comments

NEWS IN BRIEF

Malawians who Abandoned Israeli Farms Deported

The Malawi government says Israel has deported 12 Malawian workers…
Read more...

Last Witness Testifies in Matemba’s Case

The Anti-Corruption Bureau (ACB) has finished parading witnesses in the…
Read more...

Owaganizira Kupha Awamanga

Apolisi amanga abambo atatu - a Gift Banda a zaka…
Read more...

Court Adjourns Chisale’s Case

Principal Resident Magistrate Rodrick Michongwe has adjourned to a later…
Read more...

NBS Yawonjezera Makobili a Chikho

Bank ya NBS lero yalengeza kuti yakweza ndalama zomwe imapereka…
Read more...
Go to top
JSN Time 2 is designed by JoomlaShine.com | powered by JSN Sun Framework