Loya Wati Athandiza Mayi waku Mchinji Yemwe Apolisi Anamumanga Pamodzi ndi Khanda Lake

Loya wina Alexious Kamangila ,wadzipereka kuti ayimira mwaulere mayi wa zaka 30 ku Mchinji, yemwe wakhala akusungidwa ndi a polisi pamodzi ndi mwana wake pa mlandu wonyanyalira mwamuna khanda.

A Kamangila, omwe ndi mphunzitsi ku univesite ya Malawi, ati atawerenga nkhani ya maiyu pa Zodiak Online aganiza zomuimilira kuti athandizire chilungamo pa nkhaniyi.

A Matilda Chirwa, omwe pano ali pa belo, dzulo anakawonekera ku khothi komwe wachiwiri kwa Magistrate Anne Simwaka wayimitsa mlandu-wu mpaka lachisanu sabata ya mawa pofuna kulola oyimira boma pa mlanduwu kuti abweretse mboni.

Pakadali pano, magistrate Simwaka wagwirizana ndi pempho la loya-yu kuti mayiyu akamuwunike achipatala, ngati kumangidwa kwake sikunasokoneze kaganizidwe kake komanso umoyo wake poti anali atachira chakumene.

Read 2246 times

Last modified on Thursday, 10/08/2023

Login to post comments

NEWS IN BRIEF

Last Witness Testifies in Matemba’s Case

The Anti-Corruption Bureau (ACB) has finished parading witnesses in the…
Read more...

Owaganizira Kupha Awamanga

Apolisi amanga abambo atatu - a Gift Banda a zaka…
Read more...

Court Adjourns Chisale’s Case

Principal Resident Magistrate Rodrick Michongwe has adjourned to a later…
Read more...

NBS Yawonjezera Makobili a Chikho

Bank ya NBS lero yalengeza kuti yakweza ndalama zomwe imapereka…
Read more...

Passport Fees Reduced; E-system Restored

The Department of Immigration and Citizenship Services says it has…
Read more...
Go to top
JSN Time 2 is designed by JoomlaShine.com | powered by JSN Sun Framework