Loya wina Alexious Kamangila ,wadzipereka kuti ayimira mwaulere mayi wa zaka 30 ku Mchinji, yemwe wakhala akusungidwa ndi a polisi pamodzi ndi mwana wake pa mlandu wonyanyalira mwamuna khanda.
A Kamangila, omwe ndi mphunzitsi ku univesite ya Malawi, ati atawerenga nkhani ya maiyu pa Zodiak Online aganiza zomuimilira kuti athandizire chilungamo pa nkhaniyi.
A Matilda Chirwa, omwe pano ali pa belo, dzulo anakawonekera ku khothi komwe wachiwiri kwa Magistrate Anne Simwaka wayimitsa mlandu-wu mpaka lachisanu sabata ya mawa pofuna kulola oyimira boma pa mlanduwu kuti abweretse mboni.
Pakadali pano, magistrate Simwaka wagwirizana ndi pempho la loya-yu kuti mayiyu akamuwunike achipatala, ngati kumangidwa kwake sikunasokoneze kaganizidwe kake komanso umoyo wake poti anali atachira chakumene.